15/05/2026
THE MANIPULATED QUEEN
Chapter 103
Anali muofesi yake pamene amalandila foni. Anatenga ndikuyankha asanawone amene amayimbayo.
"Yes?"
"Ndibwera ndizakutenge 7 o'clock."
"Oh Zack?"
"Tiziti you didn't save me kapena ndi dala?"
"Ukufusa mafuso achoziwaziwa bwanji?"
"With you it's always different."
"Sindinaone poyankha."
"Better."
"And as for the date I think ndibwera ndekha. Don't bother kuzanditenga."
"Koma it could have saved us time."
"But it's good I show up."
"If you say so then. No problem."
"Send me the details."
Anasiya foni yake patebulo nkumapitiliza kugwira ntchito.
Ataweluka anakakumana ndi Zack. Pamene amafika anthu ena amamunjambula chapatali. Atalowa anaona kumene kunakhala Zack.
Zack anayimilira akumwetulira. Anakamukokera mpando kuti akhale. Atakhala anapasana moni kenako kunabwera waiter amene anatenga oda yawo.
"Am lucky." Anatero Zack akumwetulira.
"Ndi chani?"
"Ukuona atola nkhani amene azungulira dela ili? Am the second man to be with you in public. Oyamba ndi Rod."
"That."
"Apa wapezesa anthu chokamba. I believe wina afusa kuti tiziti wasiyana ndi Rod?"
"If you want money. Apase anthu nkhani yoti azikamba. Pamene iweyo ukupanga ndalama. Big money."
"Zimene umakamba pano ndizokhuza ndalama. Anyway this date is organized by me ndiye anything from work is not accepted. I want to know you Molly."
Molly anamwetulila ndipamene kumabwera waiter kuzasiya zinthu zawo.
"And be honest with me."
"Ndiyesera."
"I know your name. Koma I want to know about your family."
"Nkhani yomwe wayambisayi ndiyovuta."
Anatero akupumira mwamba.
"I just want to know you."
"Ndilibe aliyense."
"What do you mean?" Anafusa mokhuzika.
"I lost my mother 5 years ago."
"Oh am sorry. This is bad news..."
"No it's okay actually. Ndiwe oyamba kundifusa za moyo wanga. Time has passed though. Pena zimamveka ngati ndi dzulo. She just... she just changed poyera yera and lost her self. She couldn't recognize me. Nthenda yawo inafika paja povuta and unpredictable. At the same time I lost my friend."
"Which friend."
Anaganiza kaye asanayankhe.
"I lost Stella." Anyamba kuganiza za memory yake.
"What do you mean? Ukufuna kundiuza kuti anayamba ndi mai ako kenako Stella?"
Molly anamuyang’ana kwakanthawi.
"They died tsiku limozi. I was alone that time. Passing through pain imene sindingafotokoze. Lucky Stella's funeral inapangidwa ndi akwawo and it took days kuti malilo achitike. But as for me. I hade to do everything on my own. Pamalilo amayi anga tinalipo ochepa. Some were her friends enawo sindimawaziwa. I was young that time and I didn't know how to handle such cases. Then pamene ndimabwerera it was the sale day Stella was supposed to be buried. I was tired of everything around me. Losing my friend and my mother was a big slap. Koma lucky Rod was my distraction you know."
"Rod, mwamuna wa the late Stella?"
"Late?" Amafuna asutse.
"Yes."
"You too mwakhala muli talk of the town."
"He was broken to tell you. Sindinaonepo mwamuna akulira for nkazi. I can tell you mpaka lero he is still mourning his wife." Anatero chokumwa ndikumwa.
Zack anaseka.
"Usandinamize. Mene mumachitila muja? I thought you two are a thing?"
"Honest mene anthu mumamuomera Rod ndi imeyo. You have a bad conclusion. I can tell you kuti kwa ineyo he is my brother. And am his sister. That's it. I don't know zinachitika motani koma as years went by. I loved him as a relative. "
"So you have being in love? Umatha kusiyanisa. Who is the lucky guy?"
"Enough about me. Let's hear from you."
Zack anaseka.
"This is nice. Mene umandikanila muja? I never thought your friendly."
"Tell me, unayambapo waba ndio mumphika?"
Zach anaseka mapaka anthu anayamba kuwachewukira.
"Limenero likhale fuso? I thought undifuso la decent."
"Ngati?"
"How many girls I have dated."
"Limenero ndiye la mfundoless."
Anadulidwa ndi foni ya Molly imene imaitana.
"Ndiyankhe nao."
"Okay."
Anayankha foni ija.
"Rod?" Anadikira kuti ayankhule koma kunali chete.
"Rod?"
"Am scare."
Anayimilira mwachangu.
"Ulikuti?"
"It.. it's okay.. am fine."
"Uli kuti?"
"Am scare Molly. I can't do it."
"Chani?"
"Work."
Anadekhetsa ntima wake ndikukhala pasi.
"Am scared to go to work. They will call me names."
"Rod wadya chani?"
"Ndadya."
"Just go and sleep. Ndibwera mawa kunyumba kwako."
"Akuti ndikayambe mawa."
"Akuti? Ndani?"
"Molly..."
"Don't think about it. At least waganiza zobwerera kuntchito. That's the best thing to do."
"Okay then. Good night."
"Good night."
Anadula foni.
"Rod?"
"Yes."
"Tinali pati?"
"Ndio"
Anasekera limozi.
Atamaliza kucheza ananyamuka nkumapita. Anakamusiya Molly kunyumba kwake.
Molly anakalowa nyumba nkumakakonzekera zoti agone.
Mawa lake anachita kuzusidwa ndi antchito. Pamene amadzuka anawona wantchito atalowa kenako anamuona Solo akulowa.
"What is happening?" Anafusa akuyang'ana wantchito wake kenako nkuzamuyang'ana Solo uja.
"And you ukuzatani kuno?"
"Get out." Anatero Solo akumuwuza wantchito uja. Wantchitoyo anamuyang’ana Molly.
"You can go."
Anateluka nkuwasiya awiliwo.
"And you?"
Solo anatulutsa foni yake nkumuonesa chithuzi koma akuoneka okwiya.
"Wayamba izi?" Anafusa akumulozera pafoni.
"Oh please."
"Ndiwe hule eti?"
Molly anaseka.
"You couldn't wait for my baby to be born and wayamba kale kuyenda ndi amuna. Ena did he touch you?"
"Ndilibe nthawi yokongana ndi iweyo. What's this-"
"Molly I told you you are mine and no man-"
"Tuluka."
"Am talking!"
"And am commanding! Get out!" Anatero akuvunga zofunda zake ndikuyimilira.
"Get out! You know what? I don't want to see you ndikamatsegula maso anga or you will regret it. And I mean it Solo. Get out!"
Solo anali atakwiya koma akupumira mwamba. Anayamba kumuyandikira Molly koma anamuona akutsegula drowa nkutulusamo mfuti.
"Get out."
Anayang'anizana kwakanthawi.
"It’s not over." Anatuluka nkumenyetsa chitseko.
Molly anatenga foni ndikuyitanisa antchito onse. Anawachenjeza za Solo.
"Amene azamulole amene uja kulowa kuno. Azaziwe kuti ntchito yamuthela. Are we clear?"
"Yes Madam."
"Good."
Comment