16/07/2026
NANKUMBA AKUSIMBA LOKOMA NDI NTCHITO YOSAMALIRA CHILENGEDWE
Alimi a kwa Mfumu yayikulu Nankumba akupha makwacha ndi pulojekiti ya *KUSAMALA* yomwe yawaphunzitsa za kusamalira za chilengedwe, komanso upangili wa kapezedwe ka ndalama kudzela mu Nkhalango.
Kudzela mu upangili wa *KUSAMALA* anthu m'delari akuchita ulimi wa kufula uchi, komanso wanthochi womwe ukuwabweletsela ndalama zochuluka.
Alimiwa akuthanso
kupanga
juice, vinyo, tea, ufa wa phala, komanso sopo, kuchokela mu mbewu zachilengedwe monga chidede, chammwamba, moringa, ndi zina.
Izi zadziwika lachinayi, pomwe Khonsolo ya Mangochi imakhazikitsa Committee yosamalira Nkhalango mdelari 'Local Forest Organizations'.
Pulojekiti ya *KUSAMALA* inakhazikitsidwa kwa Nankumba mu chaka cha 2022, ndipo ikuyendetsedwa ndi bungwe la Institute of Agriculture and Ecology, molumikizana ndi Khonsolo ya Mangochi, ndi ndalama zochokela ku Welt Hunger Hilfe.
M'modzi mwa alimi , a Biston Mtonga, ati akupha makwacha ndi ulimi wa nthochi, potsatila mbewu zomwe anapatsidwa zaka zitatu zapitazo.
"A KUSAMALA anandipatsa mbuto zitatu. Pano ndili ndi mipata yopitilira 200, ndipo ikumandipatsa ndalama zoposa two hundred thousand ndikakolora," atelo a Mtonga.
Nkulu wa Bungwe la Institute of Agriculture, a Rose Bell ati chikhazikitsileni nchito yosamalira chilengegwe kwa Mfumu Nankumba, Nkhalango zambiri ku delari zabwelera nchimake.
"Anthu ambiri apeza zochita, zomwe zapangitsa kuti nchitidwe wodula mitengo uchepe." Atelo a Bell.
Nkulu wa Khonsolo ya Mangochi, a Eliasa Sausande apempha Mabungwe ena kuti atengele chitsanzo cha *KUSAMALA* ndi cholinga choti ntchito yobwenzeletsa komanso kuteteza chilengegwe itheke ku Mangochi.