18/08/2026
Wachiwiri kwa Nduna yowona za chilengedwe a Chipiliro Mpinganjira yapeleka ndalama zokwana K500,000 kwa Duwana Muhammad kaamba ka mbiri yake ya maphunziro yomwe yalimbikitsa achinyamata ndi anthu ena.
Naye mkulu wa bungwe la Malawi Bureau of Standards a Symon Mandala sanachitire mwina koma kupeleka ina K500,000 kwa Duwana kaamba ka nkhani yake yomwe inawakhuza.
Izitu sizinathere p***a, pomwe mlembi mu unduna owona za masewero a Jasmeson Ndalama apeleka ndalama ina yokwana K200,000.
Pakadali pano mkulu wa Banki ya Standard a Philip Madinga alonjeza Duwana kuti amutsegulira akaunti ya maphunziro yomwe izisunga ndalamayi.
Izi zachitika lero, pa msonkhano wokambilana za a chinyamata *National Youth Summit* ku Lilongwe.
(Copied: Malawi).