13/08/2024
BEHIND THE MIRROR
CHAPTER 2
"chabwino sindikufuna zambiri ayi, poti fees yomwe amalipira iyeyu ukuiziwa, ndipo wafuna ndi iwe kuti asiye school osati inenso, ndiyeno ndikufuna fees yanga yomwe ndalipira ku school term ino bas k350,000, Pompano".
Charles anangoti kakasi, kusowa choyankha apa ngakhale ndalama yoti akagule chakudya analibe, anali ndi maganizo ndalama yonseyi ndichoka nawo kuti......
"komano sir mwaulemu wake bwanji mutandipasako mpata pang'ono kuti ndikhale ndikusaka ndalama imeneyo".
"ndikuti ndikuifuna Pompano osati za mawazo."
"ndalama ndi yambiri sindingaipeze lero ndi lero, ndamukonda mwana wanu sindingamusiye chifukwa mwandilamula zoti ndibweze ndalama ya fees ayi".
"ukuziwa Usamandilakhule zachamba apa wamva, ndiye iwe Brenda mwamuna wako akudikira kuti alipire ndalama apa iwe pita mnyumba uzikapakira zinthu zako chilichonse chomwe chili chako uchose mnyumba muno chifukwa ukachoka suzabweranso".
"koma dad".
"Ukundiziwa sindikufuna kubwereza zinthu kawiri,panga zomwe ndakuuza Pompano".
"koma amuna anga, musapere chigamulo mwachangu musaiwale kulinso mawa".
"ndiye kuti zikukusangalasani zomwe wachita iyeyu eti, kapena munapangana, ndizomwe mumapanga mukasala pakhomo pano".
"ayinso chabwino m***a kupereka chigamulo chomwe mukufuna basi simundimvanso ndikuikira mulomo nkhani imeneyi".
"Brenda panga zomwe ndakuuza ndipo mnyamata iwe utha kupanga zomwe ndakuuza, ukachedwa police ibwera kuzakutenga ndipo ndili serious".
Brenda misonzi inayamba kugwa kwinaku akupita ku chipinda kwake kukapakira zinthu zake.
"Mr muli apa ndilore ndisake ndalama, ngakhale mundiitanire police sizipangisa kuti ndalama ikuluke pomwe ine ndilibe apo pokha ndiye ndikunamizani".
"ukupanga zibwana ndi ine eti?, ukuyenda ngati ndikuseka kapena?,".
"ndikuziwa kuti nkhani ndiya serious, ndipo apa ndili serious, chonde ndimveseseni mwina Ndikanakhala kuti ndikukana zoti mimba si yanga bwenzi mukukamba za police apa ndavomera komanso ndalama yanu ndikupasani".
Brenda anapamaliza kupakira zinthu zake anabwelera pa sitroom paja.
"well mnyamata, Brenda lero sakugona Kuno umunyamula kupita naye kwanu, ndikupasa week imodzi, ndiye ndikuuze palibe komwe ungathawire".
"palibe komwe ndingapite, Zikomo kwambiri pondimvesa".
Charles ndi Brenda Anatengana kupita kwawo.
Kanyumba komwe amakhala Charles ndi mzake Micheal kanali kakang'ono kopanda chipinda nkomwe.
Micheal anamutengera, mzake Charles pambali.
"Charles apa Brenda yemwe ndi nkadzi wako wabwera mnyumba muno koma Pali vuto limodzi".
"vuto lanji?,".
"Charles ukunena chilungamo sukuziwa vuto lake, tilipo anthu atatu sopano, malo ogona zikhala bwanji?".
"apa zinthu zavuta kale komanso ndilibe ndalama yoti ndingathe kukhala pa dekha please ndimvese, zikayamba kuyenda ndizasamuka".
Micheal anapumila mmwamba....
"chabwino ndakumvani pamenepo".
Charles analowa mnyumba kumuitanira Brenda panja...
"Charles ndiye makhalidwe ake tizikhala motani nyumba kakang'ono ngati kameneka".
"well, poti zavuta tizikhala movuta momwemo and ndikupepha kuti chomwe uzipase ulemu wekha ukuona kanyumba kakang'ono komanso tili anyamata awiri".
"Osadandaula Charles, ndikuziwa zoti muli ananyamata awiri, sindipanga zibwana zilizonse".
"ndimamukonda kwambiri Brenda".
"inenso Charles ndipo ndalimba mtima kuti tivutikire limodzi basi pa ulendo umenewu".
Awiriwa anayang'anizana, kupasana kiss...
____
Emily anadabwa mzake Brenda sakumuona komanso ku school sakupita.
Iye anaganiza zoti apite kwawo akamuone, mmaganizo mwake amati mwina akudwala.
Atafika anagogoda pakhomo.. Ndipo anatuluka anali mayi ake a Brenda apa Bambo ake anali ali ku ntchito.
"Emily Ulipo koma ndiye ungaziwe kusowa".
"ndilipo amayi kungoti mukuziwa kale ndiza school zaku zija basitu mpata ukusowa".
"paja ana a school ndinaiwala lowantu nanga".
"mmmmhhh mwina nditha kulowa amene ndikufuna palibe".
"unena Brenda?".
"eya kudabwa ku school sakubwera".
"kodi sanakuuze zomwe zachitika".
"ayi sindikuziwa kalikonse".
"takhala apa ndikuuze".
Emily anakhala pampando omwe unali pakhonde.
"mzako Brenda, ali ndi mimba moti ndikunena pano Bambo ake anam***amangisa ali ku banja kwawo kwa mwamuna wake.
"mimba Brenda?, sozakhala bwino ngakhale pang'ono, Zikomo kwambiri amayi pondiziwisa ndimusaka komwe ali ndikamuone".
"Zikomo".
"basi ndinyamuke".
"uyende bwino, mwana wanga".
Komatu zonsezi zoti Brenda Ali ndi mimba Emily ankaziwa ndithu, koma zoti ali kwa mwamuna wake samaziwa kalikonse, anakoza tsiku loti apite akamuone.
___
Patatha sabata ziwiri pomwe Charles anauzidwa kuti abweze ndalama zikwana k350,000, kwa Bambo ake a Brenda.
"mwamuna wake a Brenda sakufuna kubweresa ndalama zanga akufuna ndigwirise ntchito mphavu sopano kapena akuyesa ngati ndaiwala".
"dekhan amuna anga munthu uja zikuonesa ngati alibe ndalama akusakabe".
"ndimupitira kwawo komweko".
"mukuziwa komwe amakhala?".
"eya, ndinamufufuza kale".
Mmawa wake Cha mma 10 o'clock Mmawa Bambo a Brenda anakatenga police ulendo wa kwa Charles.
"Charles tuluka apa chanu". Bambo a Brenda Anakuwa akumenya Chiseko.
Anakuluka anali Brenda koyamba Kenako Charles.
"police nyamata wake ndi ameneyu mtengeni".
Kuti azimumanga Brenda anathamanga kuima kusogolo kwa Charles.
"madala ngati mukufuna kupanga Charles mumange limozi ndi ineyo.......
Ikupitilira.........