08/06/2024
NTCHITO ZOPITITSA CHIPANI PA PATSOGOLO ZIKANALI MKATI
Bwanankubwa (DG) wa Lilongwe urban, bambo M***a Saidi Kunkhokwe ali ku Chigwiri Ward komwe akupereka uthenga wabwino wachiyembekezo kwa ma membala achipani cha DPP.
Bambo Saidi ati m'nthawi imene DPP inali m'boma kuyambila nthawi ya malemu Prof. Bingu wa Mutharika (nzimu wao upitirire kuunsa mu mtendere) komanso mu nthawi ya President Prof. APM chilichonse chinali m'chimake.
"Lero tikuchitila umboni kuti DPP motsogozedwa ndi President wathu Prof. APM inakwanitsa kupereka utsogoleri wabwino. Munthawi ya DPP panalibe m'malawi amene anatisiya chifukwa cha njala komanso DPP inkaonetsetsa kuti chitetezo chikhale m'chimake" atero a DG, Hon Saidi
Ena mwa anthu amene anali nawo pa msonkhanowu ndi monga Mr Andrew Kowedza, Mr Namakhwa komanso akulu akulu ena amu committee ya Lilongwe Urban District. Masapota achipani cha DPP ati okondwera ndi momwe a DG akugwirila ntchito yotukula chipani mu Lilongwe District.
DPP woyeee!!!!!!
Prof. APM woyeee!!!!!!
Hon AG woyeee!!!!!!
Hon RG woyeee!!!!!!
Hon DG woyeee!!!!!!